10/05/2025
Hello, Hello Azibale anga okondedwa kuno kwathu Ku Kapiri,
Kkkkk tasowanatu kkkkk 😃😃😃 Ndilipo ine Mlongo wanu , mwana wanu ndipo zazikulu zikuchitika ndipo zichitika ndithu osadandaula, osaopa koma chinthu chimodzi tisunge umodzi paja Nkhondo simanga mudzi ndie zambiri zizikambidwa koma osabweza mau oipa kwaoipawo pewani ndithu azibale anga.
Komano lero ndine munthu osangalala kwambiri kuona ndikuva kuti nkhani imene anzathu ochita malonda pa Msika wathu yatha kubwalo la Milandu Ku Lilongwe ndipo pali chiyembekezo kuti tsopano maloto athu ikhala ndi Msika wamakono aphelezera. Ndipo ndithokoze anzathu ochita malondawa potengela nkhani Ku bwalo lamilandu kuti apeze thandizo la chilungamo pa Malo amene Iwo amachitilapo malonda ndipo izi zasonyeza kuti ngakhale chitukuko chili chofunika komabe tisamafele mmazila pofunafuna chilungamo chammene ndondomeko ya chitukuko chiliri.
Ndiloreni ndithokoze Gogo Senior Chief Dambe chifukwa chosatopa kulondoloza nkhani imeneyi kuti chilungamo chioneke ndipo Agogo ndi Mafumu Anu onse osaiwala a Group Village Nthema mumve kukuyamikilani simunatope pofunitsitsa kuti chilungamo chioneke chimene chinatchinga chitukuko chofunikilachi mdela lathu. Ambuye akudalutseni kopambana.
Achinyamata ndi mzika zonse kuno Ku Kapiri nanuso munayesetsa kutilimbikitsa kutiwunikila komaso kuyenda nafe posayang'ana zipsyinjo zimene zinalipo tiyeni tipitilize kupanga zinthu zotele zimene ndizothandiza kutukula Dela lathu. Ine ngati Phungu wanu ndine osangalala koposa. Ndipo Ambuye akudalutseni kopambana.